spot_img
26.4 C
New York
Tuesday, July 2, 2024
spot_img
spot_img

Kulira kwake ndiye nkumatani abale?- UTM

Chipani cha UTM chati imfa ya Soldier Lucius Banda mnjowawa kwambiri maka pomwe chipanichi chikulirabe mtsogoleri wawo a Saulos Chilima.

Banda anali mkulu okopa (Campaign Director pachingerezi) anthu mchipani cha UTM.

Mneneri wa UTM a Felix Njawala wati ngati chipani sakudziwa kuti nkumatanino ndi momwe imfa yatengera akuluakulu ake motsogozana.

“Pomwe a Chilima ankachokera ku South Korea posachedwa, adadzera ku South Africa kukamuona Lucius Banda.

“Akuluakulu a chipani angapo akhalanso akukamuona. Sitinaganize kuti zithera chonchi. Kulira kwake ndiye nkumatani abale?” a Njawala awuza Times 360.

Related Articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -

Latest Articles