spot_img
spot_img
20.3 C
New York
Wednesday, September 18, 2024
spot_img
spot_img

Ife za mgwirizano sitikupanga nawo, tizayima patokha- Nankhumwa

Chipani chotsutsa boma cha Peoples Development (PDP) chati chidzatenga nowo gawo pa chisankho cha 2025, poyima paokha.

Mtsogoleri wa chipanichi a Kondwani Nankhumwa anena izi pa msonkhano waukulu wa chipanichi ku Blantyre.

M’mawu awo ati anthu ena akhala akuganiza kuti chipani cha PDP chilibe chikoka kumadera a mdziko muno koma lero azionela okha.

Iwo ati kudzera pa msonkhanowu pomwe pabwera nthumwi zochokera maboma onse mdziko lino, ndichitsimikizo kuti chipanichi ndichamphamvu choncho sakuganiza kuti ndikoyenera kugwirizana ndi zipani zina.

Mthumwi pa msonkhano wu zatsimikiza kuti a Nankhumwa ndiwo mtsogoleri wachipanichi kwa zaka zisanu zikubwerazi ndipo iwo adutsa popanda opikisana naye.

Nthumwizi zasankhanso a Rose Sagala kukhala wachiwiri kwa mtsogoleri wachipanichi pomwe a Semion Phiri ndiwo awasankha kukhala mlembi wamkulu wachipanichi.

Related Articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -

Latest Articles