spot_imgspot_img
Sunday, March 30, 2025
spot_img
spot_img
HomeLatestIne sindikuchoka m'boma-Chakwera

Ine sindikuchoka m’boma-Chakwera

Mtsogoleli wa dziko lino Dr. Lazarus Chakwera wanenetsa kuti sachoka m’boma kudzera pa zisankho za pa 16 September.

Dr. Chakwera ati salola kuti anthu omwe amaba ndalama ku Reserve Bank komanso ku nyumba zaboma kuti abwelelenso m’boma.

Iwo anena izi pomwe amatsekukira msonkhano wa masiku awiri wa aluso la ntchito zamanja (2025 National Tevet Conference).

Dr. Chakwera ati pakadali pano iwo atseka makomo onse omwe anthu amabera ndalama zaboma.

Mtsogoleli-yu watsindika kuti kutsekaku kuthandiza kuti ndalama zomwe zimabedwa zigwire ntchito yomangira sukulu, misewu ndi zina. (TWR)

RELATED ARTICLES

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisment -

Most Popular