spot_img
spot_img
22.8 C
New York
Monday, September 16, 2024
spot_img
spot_img

Ana ama 2000 sima level anu- Wikise

“Inu anthu azaka izo! Ana ama 2000 sima level anu, mungothapo ndalama chabe. Inuyo ndinu okwatira ndalamazo kadyeni ndi akazi anu kunyumba.”

Umenewo ndiye uthenga waukulu mu nyimbo yatsopano ya Wikise yomwe akuyitcha kuti, Amolo.

Amolo ndichidule cha a Molotoni, bambo wa mvula zakale, obadwa malemu Kamuzu Banda akadalamula.   

Bamboyi wapeza ndalama za ngongole ya NEEF, koma m’malo mochita chitukuko ndi ndalama ya ngongoleyo, akupezeka kuti akuseweletsa ndalamazo malo azinjoyi ndi ana obadwa Facebook itayamba.

Njonda yachimimba chake Amolo-wo, munyimbomo yachitidwa chipongwe kujambulidwa malichocho, ndipo msungwana wachisodzerayo wawakakamiza kuti amulipire 20 million kwacha kuti asawayalutse.

Nanga a Molo akanatani? Mapeto ake apelekadi.

Related Articles

LEAVE A REPLY

Please enter your comment!
Please enter your name here

- Advertisement -

Latest Articles